Matigari
Gawo 19
Palibe boma lililonse, ngakhale litakhala lankhanza chotani,
lomwe linakwanitsapo kuletsa zonena za khamu la anthu
ambiri. Nyimbo zija zinafala paliponse ngati moto wolusa.
Zinkaimbidwa m'midzi yonse. Anthu ankaimba nyimbozi usiku
ndi usana. Nthawi zina ankayamba ndi nyimbo ya wophunzira
uja:
Ngakhale mutiphe,
Chipambano ndi chathu!
Chipambano ndi chathu!
Kenako ankayamba kuimba nyimbo ya Matigari ma Njiruun-
gi:
Ndionetseni munthu
Yemwe dzina lake ndi Matigari ma Njiruungi,
Yemwe akamayenda m’mapazi mwake m’malira maberu.
Komanso zipolopolo, ngindee!
Komanso zipolopolo, ngindee!
Koma kodi Matigari ma Njiruungi anali ndani kwenikweni?
202