Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 199

Matigari oweruza milandu, oyang'anira ndende ndiponso akuluakulu ena a bomanu, ndikufuna kukuuzani kuti mwangotsala madzi amodzi, masiku akucheperani! Ndibweranso mawa. Ife ndi an- thu omenyera ufulu wadziko lathu omwe tinapulumuka: a Matigari ma Njiruungi! Ndipo enanso ambirimbiri a ife tikubad- wa tsiku ndi tsiku. John Boy, ndikufuna ndikuuze kuti usadzagonenso m'nyumba yanga ija. Tiona kuti mwamuna ndi ndani pakati pa iweyo ndi ineyo. Sindikunyengerera, ubweza zanga zonse!" Anthu onse anali m'chipinda muja anayamba kuwomba m'manja. Kwa kanthawi, apolisi anakhala ngati akuopa kupita kukamugwira. Koma kenako anabwera n'kumumanga unyolo ndipo anakamuponyera mumdima. Khamu la anthu anali m'chipindacho linayamba kuwawooza apolisi aja. Kenako anayamba kuimba kuti: Ndionetseni munthu Yemwe dzina lake ndi Matigari ma Njiruungi, Yemwe akamayenda m’mapazi mwake m’malira maberu. Komanso zipolopolo, ngindee! Komanso zipolopolo, ngindee! Nduna ija inayamba kuyankhula. Inayesetsa kuti mawu ake amveke koma kuimbako kunangomiziratu mawu akewo. Ke- nako anakuwa n'kunena kuti: "Kodi si panja ndaletsa nyimbo zonse zokhudzana ndi Matigari ma Njiruungi! Tsopano ndikuletsanso maloto onse! Li- meneli ndi lamulo latsopano. Mwamva? Nyimbo zonse zaupan- du komanso maloto onse ndi oletsedwa!" 198