Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 195

Matigari a kusukuku yaukachenjede. Ndikufuna kuchenjeza ophunzira amenewa kuti mkulu wa apolisi ali pomwe pano ndipo aka- pitiriza kuyambitsa chisokonezo adziputira mavuto. Ngati mukufuna kuimba, bwanji osamaimba nyimbo zovomerezeka zomwe zili m'buku la So ngs o f a Parro t. Sindikufunanso kumva nyimbo zina zoyambitsa chisokonezo. Zimene mwamva kwa wophunzira uja ndi bodza lofuka utsi. Sukulu yaukachenjede yatsekedwa chifukwa choti ophunzira anachita ziwonetsero posagwirizana ndi chakudya chimene sukulu ikuwapatsa . . . Ndi wophunzira m'modzi yekha amene watisiya atapondedwa ndi anzake omwe amathawa . . . Koma sitinabwere pano kuti ti- dzakambirane nkhani ya ophunzirayi . . . Ndiye bwanji ndipi- tirize kuwerenga chigamulo chomwe oweruza athu odziwa ntchitowa apereka. Ndikufuna kuti muiwaliretu nkhani imeneyi msangamsanga, tamvana? Onse omwe anathawa kupolisi aja akatsekeredwa kundende ndipo akaikidwa ku alimande mpaka mlandu wawo utakaweruzidwa kubwalo lamilandu. Amenewa anaweruzidwa kuti akatsekeredwe kundende yachitetezo chokwima kwambiri mpaka nkhani yawoyi itaweruzidwa." Kenako apolisi anawatenga n'kuyamba kutuluka nawo. Munthu uja anamangidwa chifukwa chomangoyendayenda m'tauni anakodola phwete la anthu atanena kuti popeza ali ndi chitsimikizo choti kundendeko akapezako chakudya komanso malo ogona, akuthokoza kwambiri oweruza aja chifukwa cho- mukomera mtima mwanjira imeneyi. "Tsopano tifike ku mlandu wa Ngaruro wa Kiriro. Oweruza athu akhumudwa kwambiri ndi zimene munthu ameneyu wachita. Kungochokera pamene tinalandira ufulu wathu wodzilamulira, munthu wina sanayambepo watsutsa poyera lamulo limene pulezidenti wapereka. Anthu ngati 194