Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 194

Matigari Nthawi yomweyo wapolisi wina anagwira wophunzirayo pakamwa. Atangomutseka pakamwapo, pakamwa pa mphunz- itsi uja panatseguka. Mphunzitsiyo anapitiriza pamene wophunzira uja analekeza: "Tsopano ndazindikira kuti pali choonadi cha mitundu iwiri. Choonadi china chimakhala cha anthu amene akuzunza anzawo; pomwe china chimakhala cha amene akuzunzidwa! Ine sindidzayerekeza kuimba ngati parro t, mpaka ndidzalowa m'manda! Ine ndipitirizabe kuimba molimba mtima nyimbo ya chiyembekezo yomwe ophunzira opanda mantha komanso an- zeru aja amaimba." Ndiyeno pamene ankati ayambe kuimba nyimboyo, anangozindikiranso dzanja laphimba pakamwa pake. Tsopano wophunzira komanso mphunzitsi uja anatengedwa n'kupititsid- wa kwa asilikali oyang'anira ndende. Koma sanasiyebe kuchita mavuvu. Chachitik achi si chilungamo ! Kenako kuchokera paka- tikati pa anthu anali muholo muja, wina anakoleza moto wanyimbo ija: Ngakhale mutitsekere m'ndende, Chipambano ndi chathu! Chipambano ndi chathu! Nyimboyo inakolera holo yonseyo ndipo onse anaimba ndi mtima umodzi. Apolisi atazindikira kuti anthuwo afika posale- letseka anayamba kuwomba mizinga. Ndiyeno pulofesa wokha- zikika wa Parro to lo gy uja anayamba kunong'oneza Nduna Yoona Zachilungamo ija. Posakhalitsa ndunayo inayankhula mokuwa kwambiri kufika pamapeto pa mawu ake kuti: "Chete! Aliyense akhale chete! Ndangotsinidwa khutu posachedwapa kuti muholo ino mulinso ophunzira ena 193