Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 192

Matigari Lemekeza atate wako ndi amako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako achuluke Usaphe Usachite chigololo Usabe Usamnamizire mnzako Usasirire mkazi wake wa mnzako; usakhumbe nyumba yake ya mnzako, munda wake, kapena wantchito wake wamwamuna, kapena wantchito wake wamkazi, ng’ombe yake, kapena bulu wake, kapena kanthu kalikonse ka mnzako Kenako anakhala pansi ndipo apa n’kutinso oweruza a pompopompo aja akutuluka. Pambuyo pawo panali pulofesa wokhazikika wa mbiri ya Parroto lo gy uja komanso wofufuza milandu wovala chipewa choonetsa maso okha uja. Mtsogoleri wa onsewa anali mzungu wina wachikulire, yemwe anapereka chikalata chachigamulo kwa nduna ija. Ndunayo inalamula kuti anthu onse omwe anagwidwa aja apititsidwe kutsogolo kuti aliyense akamve chigamulo chomwe alandire. Apolisi anapita kukawatulutsa m’chipinda chija ndipo anawaika m’magulu atatu. "Ndikufuna kuti nonsenu, kuphatikizapo alendo athu ole- mekezeka omwe achokera ku USA, Britain, West Germany ko- manso France, muone mmene timagwiritsira ntchito malamulo m'dziko lachikhristu komanso lademokalase. Ndikudziwa mayiko ena omwe anthu opalamula milandu ngati imene apal- amula awayi amangonyongedwa kapena kuwomberedwa ndi mfuti basi. Koma kuno timaonetsetsa kuti tikugwiritsa ntchito malamulo moyenerera. Mwachitsanzo, ineyo ndine Nduna Yoona Zachilungamo, komabe nanenso ndiyenera kumatsatira 191