Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 191
Matigari
Ndalama zimene mukanamalandira zikanamakhala zokwanira
kwa inuyo ndi azikazi anu. Koma pali njira inanso yabwino
kwambiri yochepetsera chiwerengero cha anthu omwe ali
m’dziko lino. Mimba ndi zotsatira za zilakolako komanso
maganizo oipa. Ndikufuna ndipemphe boma kuti liletse kuti
anthu asakhalenso ndi zilakolako komanso maganizo oipawa
kwa zaka ziwiri. Tipempha apulezidenti kuti akhazikitse
lamulo loti anthu osauka asiye kaye kukwatira kapena
kukwatiwa chifukwa zimenenezi zikuchulutsa chiwerengero
cha anthu m’dziko muno.”
Anakwangula motero ndipo kenako anapita
n’kukadzisomeka pampando anachoka paja. Ndiyeno Nduna
Yoona Zachilungamo ija inayambanso kuyankhula.
“Dera lino ndi lodala kwambiri pokhala ndi atsogoleri
olingalira bwino ngati amenewa. Tsopano ndipemphe
wansembe wathu kuti atiwerengere malamulo khumi.
Ndikufuna nonse mutchere khutu kuti mumve malamulo a
Mulungu.”
Kenako anakhalanso pansi. Wansembe uja anatsegula
Baibulo lake n’kuyamba kuwerenga. Anawerenga kuti:
Usakhale nayo milungu ina koma ine ndekha
Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro
chilichonse
Usatchule dzina la Yehova Mulungu wako pachabe
Samalira tsiku la Sabata likhale lopatulika, monga Yehova
Mulungu wako anakulamulira. Masiku asanu ndi limodzi
uzigwira ntchito, ndi kuchita ntchito zako zonse; koma tsiku
lachisanu ndi chiwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako;
usamagwira ntchito iliyonse
190