Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Página 189

Matigari angatilembere mbiri yolondola yonena za dziko lathu kuphatikizaponso mmene tinapezera ufulu wathu.” “Nawonso mudzi womwe unapeka nyimboyi uyenera kusinthidwa dzina. Ndi mudzi wamtundu wanji womwe ungamadzitchule kuti Tram pville? Kodi kumudzi umenewo kumangokhala anthu osowa pokhala komanso aumphawi? Kodi akufuna kutiuza kuti alibe kulikonse kolowera? Ngati akufuna thandizo angoyang’ana kuchipani cholamula, komanso kwa mtsogoleri wa dziko lino Pulezidenti Ole. Ayenera kuchita zimenezi mofanana ndi mmene anthu ena onse a m’dziko muno akuchitira. Ndikufuna kulengeza pano kuti kuyambira lero, dzina la mudziwu lasinthidwa. Tsopano lizidziwika kuti Progressville. Ndiye tsopano anthu anga okondedwa aku Progressville, iwalani za Matigari ma Njiruungi. Ame!” Bwanankubwa uja anapita n’kukazidzalanso pamene anafumuka, ndipo tcheyamani wachipani cholamula cha Kiama Kiria Kirathana (KKK) anaimirira.* Tcheyamaniyu anavala malaya ojambulidwa nkhope yapulezidenti komanso chizindikiro chachipani, cha mbalame ya parro t. Pamunsi pachizindikirochi panali zilembo za KKK. Zilembo zimenezi zinalinso pakansalu kake kopukutira thukuta. *Kiama Kiria Kirathana: (Gikuyu) kuimira ‘chipani cholamula.’ “Monga ine tcheyamani wachipani cha KKK kudera lino, ndikufuna kuthokoza kwambiri kampani ya Aglo -american popereka masheya kuchipani cha KKK. Tsopano fakitaleyi ndi ya tonsefe. Tawaomberani m’manja eni kampaniyi azimayi ndi abambo! Matigari ma Njiruungi akagwere uko! Tiyeninso tisiyiretu kuimba nyimbo zotamanda munthu ameneyu chifukwa zili ngati maloto oipa! Tsopano tiyeni tisamukire kunkhani ya Karl Marx, nkhani ya ophunzira komanso ogwira 188