Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 187

Matigari ndi kadaulo pankhani yonena zoona zenizeni zosawonjezera thendo. Mkulu mukumuona apayu azimufunsa ngati munthu amene wapalamula mlandu akunena zoona kapena zabodza. Akapukusa kapena kugwedeza mutu, azidziwa zimene akutanthauza. Kodi mukudzidwa chifukwa chake nthawi zonse amanena zoona? Chifukwa amachita akafukufuku pa nkhani zambirimbiri zimene zikuchitika, amafufuza paliponse . . . Ndinakuuzanitu ine! Maso komanso makutu aboma lathu ali ponseponse. Chabwino, tsopano tiyeni tidikire chigamulo . . . " Pulofesa wokhazikika wa mbiri ya Parro to logy, mkonzi wa nyuzipepala ya Daily Parro to lo gy, mphunzitsi wa Ph.D ya Parrotology komanso wofufuza milandu wovala chipewa choonetsa maso okha uja anadzuka n’kupita kuchipinda anatsekera Matigari, Ngaruro wa Kiriro komanso anthu ena aja. “Pamene akuluakuluwa akumvetsera milandu imene anthuwa apalamula, ndipemphe bwanamkubwa watauni ino komanso tcheyamani wachipani wadera lino kuti atiyankhule mawu awiri atatu.” Bwanamkubwa watauniyo anaimirira. Iye anavala buluku ndi jekete yakhaki. Anavalanso chipewa komanso mandala aakulu zedi. Komanso anavala taye yolembedwa KKK. Buluku komanso jekete anabophayo inali yokhuthala kwambiri moti inkaoneka kuti ikumulemera. Kenako anatsokomola modzitukumula kwambiri asanayambe kupukusika: “Ndilije zambiri zoti ndinene. Anduna athu anena kale zambiri zomwe zimafunika kunenedwa. Zimene anduna athu amachita zimakhala zachilungamo komanso zolondola. Mfundo zina zimene anena tsopano ndi malamulo omwe tikufunika kumayendera. Tikachita zimenezi m’dziko muno mukhala 186