Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 186

Matigari Chifukwa choti zimenezi ndi zizindikiro za maudindo awiri akuluakulu amene ndanyamula. Udindo woyamba ndi kuwonetsetsa kuti malamulo a m’dziko muno akutsatiridwa, ndipo udindo wachiwiri ndi kuwonetsetsa kuti m’dziko muno muli choonadi ndi chilungamo. Kodi munaona mmene mkulu wapolisi uja anatulutsira mfuti yake? Tsopano yafika nthawi yoti ndikuuzeni za anthu ena omwe akuonetsetsa kuti m’dziko muno muli choonadi ndi chilungamo. Mwawaona akuluakulu avala mikanjowo? Amenewo ndi oweruza komanso maloya.” “Ineyo ndimagwirizana kwambiri ndi mawu achingerezi akuti, justice d elayed is justice d enied .* Sikuti tiyenera kungoonetsetsa kuti chilungamo chikuchitika, koma anthu ena ayenera kuona ndi maso awo kuti chikuchitikadi. Choncho ndikufuna muone ndi maso anu chilungamo chikuchitika. Ndikuganiza kuti ndine nduna yokhayo padziko lonse imene imayenda ndi anthu oweruza milandu n’cholinga choonetsetsa kuti chilungamo chikuchitika pompopompo. Akuluakulu amenewa akalowa m’chipinda mwatsekeredwa anthu apalamula milandu aja kuti akamve milandu yawo. Chigamulo chiperekedwa pompano msonkhanowu usanafike kumapeto.” *Mawu achingereziwa angatanthauze: Kuchedwetsa chilungam o n’chimodzimodzi kukaniza kuti chilungamo chichitike. "Akuluakulu amenewa athandizidwa ndi pulofesa wokhazikika wa mbiri ya Parroto lo gy, mkonzi wa nyuzipepala ya Daily Parro to lo gy, mphunzitsi wa Ph.D ya Parro to lo gy komanso wofufuza milandu wovala chipewa choonetsa maso okha uja. Kodi munthu wovala chipewayu mukumudziwa? Ndikunena uyu wavala chipewa choyerayu? Ndikudziwa kuti ambiri a inu munkadana naye kwambiri m’thawi ya atsamunda. Koma wapanoyu ndi wabwino chifukwa zimene amanena ndi choonadi ndi chilungamo. Iyeyu ali ngati mboni yaboma yemwe 185