Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 185
Matigari
wabwera pagulu ngati pano n’kumadzitukumula kuti ali ndi
chikalata cha nyumba. Chikalata chake chiti? Akuti magazi
komanso thukuta lake! Ndani angamve zakuntchini kwadzadza
ngati zimenezo! Ndi ndani amene angakhulupirire munthu
atamanena kuti ali ndi nyumba koma alibe mapepala osonyezadi
kuti nyumbayo ndi yake? Munthuyu wapalamulanso mlandu
woima pachulu n’kumadzitama kuti anapha anthu!”
"Kodi dzikoli likanakhala lotani zikanakhala kuti anthu
okhawo amene amalima ndi amene amaloledwa kudya? Kodi
dzikoli likanakhala bwanji zikanakhala kuti ogwira ntchito
akakhala kuti sakugwirizana ndi zimene owalemba ntchito
akuchita amangotenga zida n'kuyamba kumenyana nawo
m'malo mothetsa nkhani mwamtendere komanso
mwachilungamo ngati mmene ndachitira ine lero? Bwenzi pali
chisokonezo chokhachokhatu padzikoli. Ndithu bwenzi pali
chipwirikiti chenicheni! Muzikumbukira kuti, kuti dziko lililonse
liyende bwino pamayenera kukhala magulu atatu awa: olemera
monga anthu a mabizinezi komanso amakampaniwa; asilikali
ndi apolisi, monga awa akukhazikitsa chitetezowa (nonse
munaonanso mmene mkulu wa apolisi anatulutsira mfuti yake
mwaluso); ndipo gulu lachitatu ndi atsogoleri monga ine ndili
pano, kapena ansembe, komanso ena omwe nditakuuzeni
posachedwapa. Ndiye taona kuti olemera, asilikali komanso
atsogoleri ndi anthu omwe amafunikira m’dziko kuti zinthu
ziziyenda bwino."
“Ndikufuna ndikusonyezeni mmene utsogoleri weniweni
uyenera kukhalira. Ndikufuna nonse mudziwe kuti ine ndine
nduna ya zachilungamo. Mwaiona suti ndavalayi? Mukhoza
kuona kuti m’katimunso muli kajekete kena, azungu amati
kawisikoti. N’chifukwa chiyani ndavala zinthu ziwiri?
184