Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 184

Matigari Apolisiwo anapeza kuti Matigari analibe chida chilichonse, ngakhale mpeni. Komabe, ngakhale sanapeze chida, anamukwidzingabe ndi unyolo. Ankaona kuti si bwino kupereka mpata kwa Dyabolosi ngati ameneyu, yemwe zolinga zake sizinkadziwika bwinobwino. Zitangotero, alendo onse omwe anali kutsogolo kwa holoyo, anatulutsira limodzi tinsalu tawo topukutira thukuta ngati anachita kupangana. Kenako anayamba kupukuta zipumi zawo zomwe zinali zitanona bwino ndi thukuta. Iwo anaupezano mtima atazindikira kuti Matigari analibe mfuti. Apolisi aja anatenga Matigari n’kukamutsekera kuchipinda kunali Ngaruro wa Kiriro komanso anthu ena aja. Munthu yekhayo amene panalibe pagululi, yemwe anathawa kundende kuja, anali Giceru yekha basi. Kenako mkulu wa apolisi uja anabwezera mfuti yake ija m’chimake akuoneka kuti akuchita manyazi kwambiri posonyeza mantha aakulu pamaso pa gulu la anthu. Nduna ija inkaoneka kuti yasokonezeka. Inkakhala ngati ikusakasaka ulusi wa nkhani imene ingatole kuti ipitirize msonkhanowo. Kenako inatsokomola mochotsa akalungusese kukhosi. Kenako inanena kuti: “Anthu amene amakonda kuimba mlandu boma lathu adzionera okha zimene zachitikazi! Kodi akuganiza kuti boma lingamasekelele anthu ngati amenewa? Nonse mwamva zimene munthu uja wanena! Ndisakunamizeni, munthu uyuyu ndiye wapalamula mulu wamilandu. Ali ndi mlandu wopezeka pamalo a eni popanda chilolezo. Anathawa kupolisi. Wakhala akumangozungulira paliponse n’kumauza anthu kuti iyeyo ndi Matigari, zomwe ndi bodza lenileni. Kuwonjezera pamenepo, 183