Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 182

Matigari Mtsamunda Williams nayenso ndi uyo, komanso mkulu wa apolisi ndi uyo waima apoyo. Afunseni ngati zimene ndikunenazi zili zabodza. Chomwe ndikupempha m’dziko lademokalaseli ndi choonadi komanso chilungamo, zimenezo ndi zimene ndikufuna. Ndikufuna kuti chilungamo chioneke.” Pa nthawiyi n’kuti Robert Williams ndi John Boy akunong’onezanabe. Kenako Boy analemba kapepala n’kumupatsira mkulu wa apolisi uja. “Kodi inuyo ndi ndani bambo?” inafunsa nduna ija. “Matigari ma Njiruungi,” anayankha motero. Nduna ija inachita mantha. Kenako inatulutsa kansalu kopukutira thukuta kuchokera m’thumba mwake ndipo inayamba kupukuta khope yake yomwe inali thukuta lokhalokha. Ndiyeno mkulu wa apolisi uja anayankhula monong’ona kwa ndunayo. Onsewa ankaganizabe kuti Matigari ali ndi mfuti m’thumba mwake. Ankadzifunsa kuti, ‘Nanga n’chifukwa chiyani sakutulutsa manja m’thumbamo?’ Ankaona kuti kalipokalipo. Komanso ankadabwa kuti, ‘N’chifukwa chiyani akuyankhula molimba mtima choncho?’ Ankaona kuti ayenera waponda mwala. Koma pa nthawiyi sakanaombera Matigari popanda kuika moyo wa anthu ena omwe anali muholoyo pangozi, makamaka alendo ofunikira kwambiri omwe anakhala kutsogolo kwa holoyo. Choncho anadikira kaye. Tsopano Matigari anali ataima chapakatikati pa holoyo. Ndipo anthu onse anangokhala duu akumuyang’ana momusirira. Panali patadutsa zilumika zambiri kuchokera pamene anaona munthu wolimba mtima choncho! Iwo anayamba kuona kuti n’zoonadi kuti anthu omwe ankamenyera ufulu wadziko anali adakalipo. Iwo ankadziuza kuti, ‘Zoonadi eti anthu omenyera 181