Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 181

Matigari “Nkhani yanga si yaitali,” Matigari anatero, “Komanso sikuti ndi yaifupi. Ndi nkhani imene nonse mukuiona m’holo ino. Nkhani yanga yapangidwa ndi inuyo komanso ineyo. Ine ndinamanga nyumba. Ndinalima munda. Ndinagwira ntchito mwakhama kufakitale. Koma Mtsamunda Williams mothandizidwa ndi wantchito wake, John Boy, anatenga zonse n’kulemera nazo. Ndinkadziuza kuti: ‘Mavuto amene angakhalepo pakati pa wakuba ndi woberedwa ayenera kuthetsedwa ndi nkhondo basi.’ Choncho tinayamba kulimbanapo. Williams ndi John Boy anali mbali imodzi, ndipo ine ndinali mbali inayo. Kwa zilumika zambiri tinakhala tikusakanasakana. Tinkasakana kuti tione amene atayambirire kugwetsa mnzake. Choyamba ndinagwetsa John Boy. Mtsamundayo sakanachita kanthu popanda kuthandizidwa ndi wantchito wakeyu. Mtsamunda Williams sakanagwedeza maziko a nyumba yanga popanda womuthandiza. Kenako pamapeto pake nayenso ndinamugwetsera m’dothi. Ndinayamba ndi kukantha Boy, ndipo kenako ndinalikha Mtsamunda Williams. Dzulo ndabwerera kwathu kuno kuchokera kunkhalango. Ndinali ndi chisangalalo chodzadza tsaya, ndipo m’thupi mwangamu ndimamva kukoma koopsa podziwa kuti ndagonjetsa adani anga. Koma mukudziwa amene ndamupeza ataima pageti la nyumba yanga? Mwana wa Boy, ali limodzi ndi mwana wa Mtsamunda Williams. Iwo anandifunsa kuti: ‘Kodi chikalata chosonyeza kuti nyumbayi ndi yako chili kuti?’ Ndipo ine ndinawafunsa kuti: ‘Kodi mukufuna chikalata chinanso chamtundu wanji kuposa thukuta komanso magazi omwe ndinakhetsa pomanga nyumbayi?’ Iwo anakana kundipatsa makiyi a nyumba yanga, ndipo anaitana apolisi kuti andimange. Apolisiwo ananditenga n’kukanditsekera kundende. Mwana wa Boy ndi uyo ali apoyo, ndipo mwana wa 180