Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 180

Matigari ukaifunse funso limeneli ndipo ine ndinamumvera. Ndiye funso langa nali: Womanga anamanga nyumba. Munthu wina yemwe ankangoonerera nyumbayo ikumangidwa anabwera n’kulowamo. Womanga uja anayamba kugona panja, pamtetete popanda ndi denga lomwe. Telala anasoka zovala. Munthu wina yemwe sadziwa n’komwe kuti ulusi timalowetsa bwanji pasingano, anabwera n’kuyamba kuvala zovala zija. Telala uja anayamba kuvala zigamba n’kumavutika ndi usiwa. Wolima anasamalira munda wake. Munthu wina yemwe amangokolola pamene sanafese anatenga zokololazo. Iye ankayasamula chifukwa cha kukhuta, pomwe wolima uja ankayasamula chifukwa cha njala. Wogwira ntchito anapanga zinthu zosiyanasiyana. Anthu ochokera kunja komanso nthata zoyamwa anzawo magazi zinatenga zinthuzo n’kuzigulitsa. Wogwira ntchito uja anatsala manja ali m’khosi, popanda olo ndi wamtambala yomwe. Ndiye funso langa ndi lakuti, kodi choonadi ndi chilungamo chabisala kuti m’dziko muno?” Nduna yoona zachilungamo ija inaima kaye pang’ono mosonyeza kuti ikudya mutu n’cholinga choti ipeze kaye chonena isanayambe kuyankha funsolo. “Siyani kuyankhula m’mafanizo. Ngati mukufuna kufunsa funso, ingofunsani funsolo mwachindunji, m’chichewa chosavuta. Musaope chilichonse. Fotokozani momasuka mavuto anu onse ndipo ine ndikuthandizani. Munthu wamulunguyo anachita bwino kwambiri kukutumizani kwa ine, sanalakwitse ngakhale pang’ono. Mwabwera kwa munthu woyenerera.” 179