Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 179
Matigari
wa anthu monga Russia ndi China.”
Matigari anayenda molowera chapakati paholoyo ndipo
m’mbali mwake munali anthu ali ndindindi. Pamene
ankapitiriza kuyankhula, manja ake adakali m’matumba achijasi
chake chija, palibe amene anayerekeza kutsokomola,
kudzikanda kapena kupanga phokoso lililonse ngakhale
laling’ono kwambiri.
“Mwafunsa kuti, n’chifukwa chiyani anthu sakufunsa
mafunso? Ndikuyankhani funso limeneli. Kuchita zinthu
mosamala sikutanthauza kuti munthu ndi wamantha. Nthawi
ina Kambuku anafunsa Kalulu kuti: ‘Bwanawe, n’chifukwa
chiyani sunayambe wabwerapo kunyumba kwanga
kudzacheza?’ Kalulu anayankha kuti: ‘Ndakhala ndikuonapo
anthu ambirimbiri akulowa m’nyumba yakoyi, koma
sindinayambe ndaonapo ngakhale m’modzi akutuluka.’ Anthu
onse mukuwaona apawa ali ngati Kalulu ameneyu. Ali ndi
makutu komanso maso, omwe amawagwiritsa ntchito kuona
komanso kumva zimene zikuchitika pamalo amene ali. Koma
ndikufuna kuuzabe anthu amenewa kuti: Mantha akachuluka
m’dziko mumachitika zoipa zambiri. Ndiye ngakhale
ndikudziwa bwinobwino zimene Kalulu anauza Kambuku,
ndichitabe zaukadziwotche pokufunsani funso inu a Nduna
Yoona Zachilungamo. Ine ndakhala ndikuzungulira kwa tsiku
lonse kufufuza munthu woti ayankhe funso langa. Ndayenda
ngodya zonse zadzikoli pa m atatu komanso pa mitundu yonse
ya galimoto. Ndayankhula ndi asing’anga, ophunzira,
aphunzitsi komanso anthu openda nyenyezi zamakono. Munthu
wina wanzeru, yemwe amawerenga mawu a Mulungu
anandiuza kuti: ‘Pita kwa Nduna Yoona Zachilungamo
178