Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 178

Matigari ataona zimene zinachitikira Ngaruro wa Kiriro. Kuwonjezera pa kuona zimene zinachitikira Ngaruro, aliyense muholoyo anali atazunguliridwa ndi apolisi. Matigari ndi nduna yoona zachilungamo ija anaima moyang’anizana. Apolisi awiri anayamba kuchita zinthu ngati akufuna kumugwira. Koma Matigari anangoti maso ga pa nduna ija ndipo anayamba kuyankhula mokweza kwambiri moti aliyense m’chipindacho ankatha kumumva bwinobwino. Ndi mawu amphamvu ngati chitsulo, anachenjeza apolisi ankafuna kumugwira aja. Iye anati: “Tangoyerekezani kutambasura dzanja lanu n’kundigwira muone! Nanenso ndine wakale kwambiri mofanana ndi dziko lathuli.” Mawu a Matigari sankasonyeza dontho la mantha ngakhale limodzi. Kulimba mtima komanso mphamvu za mawu ake zinachititsa kuti apolisi awiri aja achite mantha n’kubwerera m’mbuyo. John Boy Junior ndi Robert Williams anayamba kunong’onezana, koma sanasiye kuyang’ana Matigari. Mkulu wa apolisi uja anapita n’kukanong’oneza nduna ija ndipo anachita zimenezi chidwi chake chili pamanja a Matigari omwe anali adakali m’thumba mwa chijasi chija. “N’kutheka kuti ali ndi mfuti. Ndiye ingomulolani kuti apitirize kuyankhula, kwinaku ife tikusakasaka njira yoti timuwomberere.” Nduna ija inayamba kukhala ngati yayamba kufufuza lilime lake lomwe linasokonekera. Italipeza inanena kuti, “Musiyeni ayankhule!” Inayankhula zimenezi mokweza kwambiri kuposa mmene zinafunikira. “Pajatu ndanena kuti aliyense amene ali ndi funso akhoza kufunsa! Boma lathuli limalemekeza ufulu wachibadwidwe. Silili ngati mayiko ena omwe salemekeza ufulu 177