Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 176

Matigari ntchito yanu! Mwina nayenso ndi mmodzi mwa anthu amene akuphunzitsa chiphunzitso cha Karl Marx m’dziko muno.” Apolisi awiri anagwira Ngaruro wa Kiriro ndipo anakamuponyera m’chipinda munali anthu ena anagwidwa aja. Zimenezi zinachititsa kuti anthu aluse n’kuyamba kukuwa mokalipa. Nthawi yomweyo mkulu wa apolisi uja anaimba wizilo yake. Apolisi anali panja aja komanso anali m’mawindo aja analowa muholoyo. Zimenezi zinachititsa kuti anthuwo akhale pakati pa apolisiwo ndipo analibe kothawira. “Pali winanso amene ali ndi funso?” Atangonena zimenezi, m’holoyo munangoti zii. Kenako anapitiriza kuyankhula ngati kuti palibe chilichonse chodetsa nkhawa chimene chachitika. “Mwina ndibwerezenso. Pali winanso amene ali ndi funso ngati?” Palibe amene anayankhula onse anangoti chete. Nduna Yoona Zachilungamo ija inapitiriza kunena kuti: “N’chifukwa chiyani simukufuna kufunsa mafunso? Nokhanso mukudziwa kuti tili ndi alendo ochokera kumayiko a azungu pano, a ku USA, Britain, West Germany komanso France. Alendo olemekezeka amenewa akuchita kafukufuku. Akufuna kudziwa mmene boma komanso chipani cha dziko lino chikuyendetsera zinthu. Akufufuzanso mmene mabungwe ena omwe si aboma akugwirira ntchito zawo m’dziko muno. Ndikufuna adziwonere okha mmene chik o m yunizim u cha kuno ku Africa chimayendera. Dziko lathu lino ndi lademokalase ndipo timaonetsetsa kuti malamulo akutsatiridwa. Choncho boma lili ndi mphamvu zochotsa munthu amene akusokoneza 175