Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 175

Matigari lamulo limene laperekedwa; chachiwiri, waphwanya malamulo awiri amene mtsogoleri wadziko lino wapereka. Waphwanya lamulo lomwe ndangolilengeza mphindi zingapo zapitazo, ndipo aliyense anamva ndikunena zimenezi. Ndinanena kuti kuyambira lero kuchita sitiraka ndi koletsedwa, ndikunama kapena? Ndinanenanso kuti m’dziko muno musadzapezekenso munthu wochita kapena kulimbikitsa anzake kuti achite sitiraka. Munthuyutu akulimbikitsa ena kuti apitirizebe kuchita sitiraka. Kuchita zimenezi ndi mwano waukulu chifukwa ndiye kuti akukana kutsatira zimene mtsogoleri wa dziko lino walamula. Kodi mukudziwa lamulo limene waphwanya polimbikitsa ena kuti asamvere zimene pulezidenti wathu walamula? Akuphwanya lamulo la sed ictio n komanso treaso n, lamulo lolimbikitsa ena kugalukira komanso kuchitira chiwembu pulezidenti. Mwina nanenso n’tafunsa: Kodi makampani angayende bwanji ngati ogwira ntchito atamasankha okha mabwana oti awalembe ntchito komanso malipiro amene akuyenera kulandira? Nanga zinthu zingakhale bwanji ogwira ntchito atamasankha okha nthawi imene akufuna kupuma komanso imene akufuna kugwira ntchito? Ngati anthu akufuna zimenezi, bwanji osangotsegula makampani awo? Bwanji osangodzilemba ntchito okha m’malo momayenda mimba tiyetiye m’mafamu komanso makampani a eni n’kumakafunsira ntchito? Kumenekutu ndi kuzerezeka kwakukulu! Munthu amene wayankhula uja wakana kugwira ntchito ndipo aliyense wadzimvera mumtolo munthuyu akutafula zimenezi. Ndi ufulu wake kukhala osamagwira ntchito, palibe angamuletse. Koma alibe ufulu wolimbikitsa ena kuti nawonso atengere maganizo ake oipawa. Kodi mungamuthandize bwanji munthu yemwe wasankha kumangokhala? Anthu aulesi ndi amene amakonda kudandaula komanso kuyambitsa mavuto. Apolisi! Gwirani 174