Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 174

Matigari wa malonda amene tikugulitsa ndipo tichita zimenezi mpaka ogulawo atavomereza pempho lathu. Chomwe tikupempha ndi choti atiwonjezere malipiro kuti tizikwanitsa kupeza zofunika pamoyo, malinga ndi mmene mitengo ya zinthu yapengeramu. Zinthutu zikukwera mtengo tsiku ndi tsiku! Tikhala bwanji ndi moyo ngati tikupatsidwabe ndalama yomwe tinagwirizana zaka 20 zapitazo, zinthu zikadatchipa! Ndalamatu zimene tikupatsidwa panopa ndi zofanana ndi zomwe ena akumapatsa ana awo kuti akadyere kusukulu! Choncho tingakonde kuti malipiro azikwera mogwirizana ndi mmene ndalama yathu ikuyendera, ikagwa pansi malipironso azikwera. Tikupemphanso kuti tizipuma Loweruka, apo ayi tizilipidwa ndalama yoonjezera monga o vertim e. Nafenso timakhala ndi zochita zathu kumapeto kwa mlungu moti sitingalole kumangogwira ntchito yapwitika. Ngati akufuna tizigwira ntchito, azitilipira. Tikupemphanso kuti John Boy komanso Robert Williams achotsedwe m’gulu la anthu oyendetsa kampaniyi ndipo pasankhidwe anthu ena kuti alomwe m’malo mwawo. Anthu awiri amenewa ndi ankhanza komanso ouma mitima ngati mfiti zazikazi. Anthu amenewa anyanya moti amaposanso anthu omwe ankatilamulira m’nthawi ya atsamunda." Atangomaliza kunena zimenezi, Ngaruro wa Kiriro anakhala pansi. Ogwira ntchito onse anawomba m’manja osati pang’ono, azibambo anaimba malikweru ndipo azimayi anabulumunya nthungululu. Nduna ija inadikira kaye kuti kuwomba m’manjako kuzizire. Kenako inati: “Mwamva nokhatu mwano umene munthuyu wageya, si choncho? Munthu ameneyu wachita zinthu zophwanya malamulo maulendo atatu. Choyamba, sanamvere 173