Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 173

Matigari Ngaruro wa Kiriro anaimirira: "Ndaima kuti ndiyankhule m'malo mwa ogwira ntchito anzanga. Ndikufuna kukuuzani kuti mkangano komanso mavuto amene tikunenawa ali pakati pa mbali ziwiri: oyendetsa kampaniyi komanso ogwira ntchito, osati ndi boma kapena chipani ayi. Pamene pakhota mchira wanyani ndi poti ogwira ntchitofe tikuponderezedwa koopsa. Timagwira ntchito yolemetsa kwa maola ambirimbiri, koma timalandira malipiro ochepa zedi. Ifeyo tikuipangira kampaniyi phindu losaneneka, mamiliyoni ambirimbiri. Koma omwe anatilemba ntchitowa ayenera kuzindikira kuti amapeza mpindu lonselo chifukwa chakhama lathu. Chigamulo chimene mwapereka pankhaniyi si chachilungamo komanso ndi chokondera. Chikungosonyezeratu kuti inuyo, a m’boma komanso chipani cholamula, muli kumbali ya kampaniyi komanso anthu ena omwe ali ndi mafamu akuluakulu m’dziko muno. Koma ndili ndi funso limodzi: Kodi boma lathu, boma la ogwira ntchito lili kuti? Ifetu sitikupemphetsa zinthu zaweni, tikungofuna tipatsidwe zinthu zathu basi. Tizilipidwa malipiro ogwirizana ndi ntchito imene timagwira. Kuti ifeyo tikhale ndi moyo zimadalira ntchito imene timagwirayi. Khama lathu ndi limene lili katundu yekhayo amene tili naye pamoyo wathu. Ife timagulitsa khama lathulo m'misika. Tandiuzeni inu omwe mumadziwa zamalonda: Ngati munthu wogula sakufuna kupereka ndalama za chinthu chimene akufuna, kodi si paja wogulitsayo amakhala ndi ufulu womukaniza chinthucho mpaka atapereka ndalama imene wauzidwa? Ndipo mungandivomereze kuti nthawi zina amakambirana, mwinanso kuchotserana n’kugwirizana mtengo umene wogulayo angakwanitse. Masitiraka amene tikuchitawa akufanana ndi zimenezi. Tikukana kugwira ntchito chifukwa ndalama imene tikupatsidwa sikugwirizana ndi mtengo 172