Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 166

Matigari “Tamvetserani ndikuuzeni chinsinsi china. Boma likudziwa kuti anthu ofuna kusokonezawa akuchita zambiri. Anthu ame- newa apeza njira zina zosokonezera mtendere m’dziko muno. Akumafalitsa mabodza, uvum i. Panopa pali mphekesera ina yomwe ili ponseponse yonena kuti Khristu wabweranso. Koma ndikufuna ndikufunseni funso: Kodi Khristu angabwere bwanji asanaululire zimenezi ophunzira ake? Mutha kuona kuti kutsogolo kuno kuli munthu wamulungu. Munthu wamulungu, chonde tawauzeni anthuwa ngati mphekesera zikumvekazi zili zoona. Kodi n’zoona kuti Yesu Khristu wabweranso?” Wansembe uja anaimirira atakwapatira Baibulo lake. Anayamba ndi kuyang’ana uku ndi uku ngati wakuba, chifukwa anali asanatsimikizebe ngati zinali zoonadi kapena ayi kuti Yesu Khristu wabweranso. Kenako anayamba kuyankhula. “Ndikuwerenga m’buku la Uthenga Wabwino wa Mateyu, chaputala 24, kuyambira vesi 23. Likuti: ” Pomwepo munthu akanena kwa inu: ‘Onani, Khristu ali kuno, kapena uko musamvomereze; chifukwa Akhristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzawonetsa zizindikiro zazikulu ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati n’kotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.’” Wansembe uja atangokwangula kuwerenga mavesiwa ana- khala pansi, ndipo nduna ija inapitiriza kuyankhula. “Mwamvatu zimene mawu a Mulungu anena! Anena kuti tisamvere aneneri onyenga, angelo onyenga komanso a Yesu Khristu abodza.” “Tsopano tiyeni titembenukire pa mfundo ina. Mphekesera yabodza imene tikunenayi inayamitsidwa ndi gulu la mbava ko- manso zigawenga zina, gulu la anthu ophwanya malamulo, 165