Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 165

Matigari omvera malamulofe sitinamvere malamulo a boma lomwe linka- tilamulira, kodi mukuganiza kuti mukanakhala muli pa ufulu lero? Muzingoyamika kuti boma lathuli likulamulidwa ndi mun- thu wachifundo yemwenso ndi Mkhristu. Tangoganizani, asilikali ena anatenga zida kuti alande boma. Zoona kulanda bo- ma! Koma mitu ya anthu amenewa imagwira? Anthu amenewa ndi oipa kwabasi chifukwa akufuna kusokoneza mtendere umene tinaupeza movutikira kwambiri. Ali mitu gwa, ati akufu- na kuti moto wa ufulu wawo usazime! N’chifukwa chiyani sankachita zimenezi nthawi ya atsamunda ija? Ndiponso ana asukulu omwe akumachita ziwonetsero panja pamaofesi a akazembe a kumaiko a azungu, ati chifukwa choti akuthandiza dziko la So uth Africa! Bwanji ophunzira amenewa osatengera chitsanzo cha pulofesa wokhazikika wa Parro to lo gy? N’chifu- kwa chiyani akulowerera za maiko ena n’kumawalamula mmene angamagwiritsire ntchito ndalama zawo? Kaya ndi ku- uma mitu kaya! Ziwathandiza chiyani zimenezi! Ndipo ndikuona kuti mtsogoleri wathu, Pulezidenti Ole, ndi wachifun- do chosaneneka ndiponso amatsatira demokalase osati pang’ono. Kodi mukuganiza kuti zinthu zikanawathera bwanji akanakhala m’mayiko enawa omwe satsatira malamulo? Kodi zikanawathera bwanji akanakhala m’mayiko omwe amathana ndi aliyense amene akuchita matukutuku kapena kuyambitsa chisokonezo? Akanawapotokola makositu! Komanso kodi mukuganiza kuti dzikoli likanakhala bwanji zikanakhala kuti amene anatenga ulamuliro ndi anthu aja omwe anatenga nkhwangwa n’kumalimbana ndi malamulo? Inde . . . dzikoli likanamamuliridwa ndi zigawenga . . . M’mawu ena likanakhala boma lazigawenga. Kodi zikanakhala kuti zigawengazo ndi zimene zikulamulira dzikoli, ophunzira onse aja omwe amachita ziwonetsero aja sakanathudzulidwa?” 164