Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 164

Matigari amalemba nkhani zabodza, muona kuti anthu amene ankamvera malamulo a atsamunda ndi amene anathandiza kwambiri kuti tilandire ufulu wathu wodzilamulira. Kodi si dzulodzuloli pamene akadaulo ophunzitsa pasukulu zaukachenjede komanso akatswiri a Parro to lo gy anapanga msonkhano? Kodi anapeza zo- tani? Malinga ndi kafukufuku amene anachita, anthu amene ankagwirizana ndi atsamunda poyesetsa kuteteza lamulo ndi amene anachititsa kuti atsamunda atipatse ufulu wathu wodzila- mulira. Posachedwapa ndalamula kuti aphunzitsiwa komanso akatswiriwa omwe ali ndi Ph.D ya Parro to logy akwezedwe pant- chito komanso kuti akhale mapulofesa. Chifukwa anthu ame- newa ndi osiyana kwambiri ndi ena aja omwe akumangoliralira komanso kumangolongolola n’kumauza anthu kuti aukire, ati ‘ee tisinthe boma,’ komanso kumalimbikitsa mfundo zo- sadziwika bwino zamayiko ena. Ife tikukana kuti ayi! Mapulo- fesa awa okha ndi amene amatsatira malamulo ndiponso ku- wateteza. Mukugwirizana nane, si choncho mapulofesa athu?” Pulofesa wa Parro to lo gy uja anaimirira. Nayenso wina anali ndi Ph.D ya Parro to lo gy komanso mkonzi wa nyuzipepala uja anaimirira. Iwo anaimba mavesi atatu kuchokera m’buku lija la Songs of a Parrot ndipo kenako anakhala pansi atagwira mabuku awowo m’manja ngati auzidwa zoti akawasiya pansi awom- beredwa. Nduna ija inasangalala kwambiri ndi kuimbidwa kwa nyim- boyo ndipo inanena kuti akapitiriza kusonyeza khalidwe labwino ngati limenelo adzakhala pandandanda wa alendo ole- mekezeka komanso kuti apatsidwa mamendulao monga a GKM (Khutu la Pulezidenti) kapena MMT (Maso a Boma) . “Ndikukhulupirira kuti mwamvetsa mfundo imeneyi tsopano,” inapitiriza motero nduna ija. “Zikanakhala kuti anthu 163