Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 161

Matigari Kunja kunali kusakudziwikabe kuti kukufuna kukhale nyen- go yanji ndipo ndi mmenenso muholoyi munalili. Simunkaten- tha komanso simunkazizira. Anthu omwe anali m’holoyo ankayankhula mong’ung’udza ndipo sankasonyeza kuti akondwa kapena akwiya. Magetsi nawonso sankawala kwenikweni ndipo munali kamdima ndithu. Palibe chomwe chinkaoneka bwinobwino. Aliyense ankangodikirira. Wansembe anatsegula msonkhanowu ndi pemphero: “Atate wathu wakumwamba, tsogolerani mtumiki wanuyu, Nduna Yoona Zachilungamo, kuti achite mogwirizana ndi chifuniro chanu. Ambuye, khazikitsani pansi mitima ya oyendetsa fakitale komanso ogwira ntchito, kuti akhutire ndi chigamulo chomwe chiperekedwe pano motsatira chilungamo chenicheni.” Pempherolo litangotha, bwanamkubwa watauniyo anadzut- sa nduna ija kuti iyankhule ndi anthu ake. Kenako ndunayo inadzuka n’kuyamba kutokota. “Ndikufuna ndiyankhule mosapita m’mbali pano. Ndiyank- hula choonadi komanso chilungamo chosatsira mchere. Ndine mzati wa bomali. Ndine mzati wa anthu onse. Ndili ngati ku- wala m’dzenje lamdima. Ndine nyale yachitukuko. N’chifukwa chiyani ndanena zimenezi? Chifukwa popanda kutsatira mal- amulo, choonadi ndi chilungamo, ndiye kuti bomanso palibe, dziko palibe, komanso mgwirizanao palibe. Kutsatira malamulo n’kumene kumasonyeza kuti dziko ndi logwirizana. Ndipo ine ndinakula ndikutsatira malamulo, moti ndinganene kuti mal- amulo ndiye kudya kwanga. Ndimatsatira malamulo, ndipo lamulo limandimvera. Ndinaphunzira zamalamulo ndipo ndimawakhulupirira kwambiri. Ndine amene ndimateteza mal- amulo masiku ano. Ndimapanga malamulo ndipo ndimaone- 160