Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 16

Matigari Kenako anamva kulira kwa sailini kuchokera kufakitale ina. Sailiniyi inkalira pa 10 koloko ndipo imeneyi inali nthawi yopumira pang’ono ntchito. Bambo uja anadziyankhulanso yekha. “Kaya masiku anonso anthu akumapuma mphindi zisanu zokha basi? Koma amaganiza kuti munthu angapumedi kanthawi kochepa ngati kameneka? Nthawi imeneyitu ndi yongokwanira kupita kuchimbudzi kukadzithandiza mofulumira komanso kukoka chingambwe pang’ono.” Iye anaganizira za masailini omwe analira nthawi yonse yomwe anali kutchire kuja. Anaganiziranso za anthu omwe anaduka manja ndi miyendo komanso ena osawerengeka omwe kwa zaka zambiri anazunzika kugwira ntchito yakalavulagaga pafakitaleyi. Anadzifunsa kuti, “Nanga bwanji masiku ano? Kodi mwina n’kutheka kuti zinthu zinasintha?” Kenako anakumbukiranso mawu omwe anamva aja. “Boma la anthu . . . ” Pamene zimenezi zinkayendayenda m’mutu mwake, ankakhala ngati akuonanso Mercedes-Benz ija, kenako anaganiziranso za apolisi anakumana nawo ali ndi galu aja komanso chipatala chija. Kodi zinthu zinalidi zitasintha poyerekeza ndi kale? Iye anaona kuti apeza yankho la funso limeneli akakafika kunyumba kwake. Ndipo anatsimikiza mtima kuti sapita kwawo pokhapokha apeze anthu ake. Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ndiyambira pati kuwasakasaka?” Sailini ija inalilanso ndipo atangoimva inakhala ngati yamuthandiza kudziwa zochita. Anadzifunsa kuti, “N’chifukwa chiyani sindinaganize zimenezi poyamba pompaja?” Anthu ogwira ntchito pafakitaleyi ankachokera m’madera onse a m’dzikoli. Kufakitaleko kunkangokhala ngati kumsonkhano wa ogwira ntchito. Munthu aliyense yemwe ankafunafuna anthu ake akanayenera kuyambira kumeneko. 15