Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 159

Matigari Gawo 17 Kumsonkhano womwe Nduna Yoona Zachilungamo inai- tanitsa kunali fumbi la anthu. Anthuwa anabwera mwaunjinji chonchi chifukwa anamva zoti ndunayi yabwera kudzathetsa mavuto omwe anachititsa kuti ogwira ntchito achite sitiraka. Nayenso bwanankubwa wa m’tauniyo anayendera midzi ingapo n’kumalimbikitsa anthu kuti akapezeke kumsonkhano womwe ndunayo inkafuna kuchititsa. Pamsonkhanowu panabweradi madoda ambiri olemekezeka. Kunabwera oimira maunduna osi- yanasiyana, achipani cholamula, ogwira ntchito kukhonsolo ya mizinda yosiyanasiyana, abusa amatchalitchi olekanalekana ko- manso mabwana oyendetsa fakitale ija. Nawonso ogwira ntchito kufakitaleyo ndiponso anthu ena okhudzidwa ndi zimene zinkachitikira ogwira ntchitowo anabwera mwaunjinji. Dzikoli linali ndi mbiri yabwino kwambiri kumaiko a azungu chifukwa chowonetsetsa kuti ufulu wa anthu sukuphwanyidwa komanso kuti mukuchitika ‘chilungamo’ chokhachokha. Chon- cho, msonkhanowu unakopanso alendo ochokera kumaiko a azungu omwe anali m’dzikoli. Anthu amenewa anakhala pamipando yakutsogolo kuti awone bwinobwino mmene mfun- do za choonadi ndi chilungamo zimatetezera ogwira ntchito! Nawonso apolisi komanso asilikali omwe anapita kukakhazi- kitsa mtendere kufakitale ija anabwera kumalowa ndipo anaima ngati akufuna kumenya nkhondo kunja kwa holoyo. Mkati mwa holoyo munali apolisi ambirimbiri. Ena anatsamira khoma ndipo maso awo ankayang’anitsitsa zimene anthu anabwera kum- sonkhanowo ankachita. Nduna Yoona Zachilungamoyo inavala suti yakuda yamizere yotuwa. Taye yake yachipani yomwe inali ndi timizere tofiira komanso tobiriwira inali itamangidwa pakhosi ndipo inkangoonekera kamfundo kake kokha 158