Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 155

Matigari zovala, amene amakolola pamene sanalime uja anatenga zovala zonse. Nthawi iliyonse yomwe wolima uja wakhetsa thukuta lake n’kupanga zinthu zooneka zoti zimuthandize, wokolola pamene sanalime uja ankabwera n’kukokolola zonse. Kenako wolima uja anapeka nyimbo yosonyeza kusagwirizana ndi zimene zinkachitikazo: Sindidzalimanso nthaka kapena kudzala mbewu, Popeza wokolola pamene sanalime amatenga zonse Ine n’kumagona kumimba kuli pululu. Sindidzamanganso nyumba, Popeza wokolola pamene sanalime amalanda zonse Ine n’kumagona pamtetete Sindidzasokanso zovala, Popeza wokolola pamene sanalime amandilanda Ine n’kumayenda chinochino Sindidzapanganso zinthu Popeza wokolola pamene sanalime ndi amene amalemera nazo Ine n’kumayenda ndi matumba obooka. Ine ndakana kukhala ngati poto yemwe amaphika Yemwe amavutika ndi moto koma osadya nawo! “Munthu wamkulu ndikuuzeni! Nkhondotu inaulika pakati pa amene amakolola pamene sanafese ndi amene amalima. Ko- ma amene amakolola pamene sanalime sanali yekha. Iye limodzi ndi antchito ake anathamangitsa amene amalima uja mpaka ku- mapiri, uyo mpaka m’zigwa; anakweranso mapiri, uyo mpaka m’zigompholera; uyo m’zigwa, m’nkhalango mpaka kuma- lekezero a dziko. Anthuwa analimbana koopsa. Chaka china- dutsa. Kenako zaka khumi. Mpakatu zaka miyandamiyanda. 154