Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 154

Matigari Kodi ndi ndani amene walakwira mnzake, pakati pa Guthera ndi Mulungu? Kodi ndi ndani amene akufunika kugwada n’kupempha mnzake kuti amukhululukire? Tandiuzeni, inu amene mumawerenga malemba: Kodi ndi ndani amene ana- lenga dziko losokonekerali?” “Samala m’bale wanga! Samala kuti usachite tchimo lomwe sungakhululukidwenso!” wansembeyo anatero akuoneka kuti wazizidwa thupi ndi zimene Matigari ananena. “Kodi ndi chi- wanda chamtundu wanji chabwera kunyumba kwanga kuno?” Kenako, atakumbukira kuti wangomaliza kumene kuwerenga Baibulo. Komanso anakumbukira mphekesera zom- we zinali ponseponse m’dzikomo, ndipo nkhawa ija in- amubwereranso. Anayambanso kukayikira. “Kodi amenewa si mayesero ofanana ndi amene Mulungu anamuyesa nawo Yobu pamene analola kuti Satana amuyese?” “Tchimo lake liti?” Matigari anafunsa mopwetekedwa mti- ma kwambiri. “Tchimo lonyoza Mulungu! Tchimo lochimwira mzimu woyera!” “Ndachimwira mzimu woyera chifukwa ndanena kuti dzikoli lasokonekera? Talekani ndikuuzeninso ndagi ina yonena za munthu yemwe amakolola pamene sanalime. ‘Munthu wina anaswa mphanje, kuphwanya zigulumwa, kuunda mizere, kud- zala mbewu komanso kumazisamalira. Munthu yemwe amangokolola asanalime analanda malowo ndipo iyeyo ndi amene anatenga zokolola zonse. Kenako munthu analima mun- da uja anamanga nyumba, koma munthu yemwe amakolola pomwe sanalime uja anabweranso n’kuilanda. Wolima uja ana- manganso mafakitale abwinoabwino koma munthu amakolola pomwe sanalime uja anatenga onsewo. Wolima uja anasoka 153