Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 153

Matigari zija sizinatseguke mozizwitsa. Anadziwanso kuti nkhani zonse zokhudza mngelo Gabrieli zinali zabodza. Koma anaonabe kuti munthu ayenera kuonetsetsabe kuti nyali yake ndi yoyaka nthawi zonse chifukwa zinthu sizidziwika. Kenako anachotsa chitsokotsoko kukhosi kwake n’kunena kuti: “Ndagi mwanenayi ndi yovuta kuimasulira. Koma Ambuye wakumwamba sachita chinthu popanda cholinga. Chilala, njala, matenda, mavuto, madzi osefukira, zivomerezi, imfa komanso milili—zimachitika ndi cholinga. Mulungu amachita zinthu m’n- jira yodabwitsa. Ndipo amaulula cholinga komanso zinsinsi zake akafuna komanso nthawi yake ikakwana. Ndife ayani kuti timuuze Mulungu zochita? Mavuto komanso zokhoma zimene timakumana nazozi ndi ziyeso. Mulungu amafuna kuti aone kupirira kwathu. Zikanakhala kuti mtsikanayo sanasiye kupemphera, Mulungu akanamuthandiza kudziwa zoyenera kuchita. Koma kodi ndine ndani kuti ndiweruze munthu wina? Komanso kodi ndine ndani kuti ndilande udindo wa Mulungu n’kumaweruza munthu chifukwa cha zimene wachita? Mwa- kumbukira nkhani ya mzimayi yemwe anapezeka ndi mwamu- na wa mwiniwake ija? Kodi Yesu anauza anthu aja chiyani ata- bweretsa mayi uja kwa iye. Am ene sanayam be wachim wapo at- ole mwala kuti amugende. Eetu! Ndiye nanenso ndingotsatira mapazi a Yesu n’kunena kuti: Munthu amene sanayambe wachimwapo at- ole mwala kuti amugende mtsikanayo. Koma mtsikanayo ndimuuza kuti: Bwereranso kwa Ambuye, yambiranso kupemphera kwa Mulungu wako. Ugwade n’kumupempha kuti akukhululukire . . . ” Mosazindikira, Matigari anaulula dzina la mtsikanayo. “Koma kodi ndi tchimo lanji limene Guthera wachita? 152