Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 152

Matigari yemwe anapangana naye. Mnyamatayo anapita kukatsegula muselo yomwe munali munthu uja komanso akaidi ena khumi. Kenako mnyamatayo anakhomanso zitseko zija ndipo anaka- pereka makiyi aja kwa mtsikana uja, yemwe anakabwezera makiyiwo m’thumba la wapolisi uja n’kumanamizira kugona. Wapolisiyo atadzuka, anapeza mtsikanayo akugonabe pambali pake. Kenako anadzuka mofulumira kuti mabwana ake asamu- peze akugona muofesi. Mtsikanayo anatuluka n’kumapita. Ko- ma chisoni chinali chitadzadza mumtima mwake. Iye anali ataphwanya lamulo la khumi ndi chimodzi lija . . . Ndiye tandi- uzani, inu amene mumawerenga komanso kutanthauzira malemba: Kodi ndi pati pamene pali choonadi munkhaniyi? Ko- di ndi pati pamene pali chilungamo? Kodi n’kuti kumene mun- thu angakapeze choonadi komanso chilingamo m’dzikoli? Chifukwatu ndikudziwa ine kuti kumene kuli mtsikanayo ali ndi chisoni chosaneneka, moti misozi ikungotsika m’masaya mwake ngati mitsinje. Kodi mundiuza zotani munthu wamulun- gu? Kodi mundiuza mawu otani omwe angapukute misozi ya mtsikana ameneyu? Kodi n’chifukwa chiyani Ambuye wa- kumwamba analenga dzikoli kuti likhale chonchi? Dziko limene anthu amene amafesa zoipa amakolola zabwino, amene amafesa zabwino amakolola zoipa! Kodi buku loyera limene mumaw- erengalo likuti chiyani pa nkhani imeneyi? Tandimasulirani ndagi imeneyi, ine yankho lake likundivuta. Tandimasulirani mfundo imeneyi, ine yandikanika kuimasula. Tandiuzeni: Kodi ndikamuuze chiyani mtsikanayo? Chifukwatu ndinamuuza kuti ndikakumana naye ndikapeza mayankho a mafunso amenewa . . . ” Tsopano wansembeyo anaupezano mtendere mumtima mwake. Ankangokhala ngati wina wamutula chimwala chomwe chinali paphewa lake. Iye anazindikira kuti zitseko zandende 151