Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 151

Matigari akumwamba komanso atate ake apadziko lapansi. Iye sankalephera kupemphera ndipo sankajomba kutchalitchi. Pa nthawi ya nkhondo yomenyera ufulu wa dziko lathuli, bambo ake apadziko lapansi anamangidwa ndi apolisi. Mkulu wa apoli- si anamuuza kuti bambo akewo akhoza kumasulidwa ngati mtsikanayo atavomera kugona naye. Mtsikanayo anakana, ndipo atate ake apadziko lapansiwo ananyongedwa. Iye anatsala ndi chiudindo chosamalira azichimwene komanso azichemwali ake. Choncho anapempha atate ake akumwamba kuti: ‘Ndithandizeni kuti ndikwanitse kusamalira abale angawa.’ Iye anapemphera n’kupemphera. Koma sanapeze chakudya choti adye, sanapeze zovala zoti avale! Choncho tsiku lina anaganiza zoyamba kuyendayenda m’tauni. Iye anayamba uhule chifukwa ankangofuna kupeza ndalama yoti agulire chakudya komanso zovala. Komabe, kungochokera tsiku limenelo, analumbira kuti: ‘Ambuye, ndithandizeni kuti ndisunge mawu anga. Kuyambira lero sindidzayerekeza kuchita uhule ndi apolisi omwe anapha bambo anga komanso ngakhale wapolisi aliyense. Ndithandizeni chonde, ngakhale kuti ndine munthu wochimwa, ndipatseni mphamvu kuti ndizitsatira lamulo la khumi ndi chimodzi limeneli!’ Dzuwa linalowa n’kutuluka, ndipo masiku anabala zaka. Kenako munthu wina anabwera kuchokera kunk- halango komwe anthu omenyera ufulu wadziko lino ankabisala. Munthuyo anapeza apolisi akufuna kulumitsa mtsikanayo galu. Apolisiwo ankachita zimenezi chifukwa ankamufuna mtsi- kanayo. Koma mtsikanayo anatsimikiza mtima kuti sangayere- keze kumayenda ndi apolisiwo. Munthuyo anapulumutsa mtsi- kanayo. Posakhalitsa, munthuyo anatsekeredwa m’ndende. Mtsikana uja anapita kwa wapolisi uja n’kukadzipereka kwa iye. Kenako wapolisiyo anagona tulo tofa nato. Mtsikanayo anaba makiyi a ndendeyo n’kukawapereka kwa mnyamata wina 150