Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 150

Matigari “Moti mulibe vuto lina lomwe mungakonde kuti ndiku- thandizeni . . . mwachitsanzo kusowa zovala, kapena malo ogo- na?” “Ludzu komanso njala yanga si ya chakudya kapena cha- kumwa. Njala komanso ludzu limene ndili nalo ndi lokhudza nkhawa zanga. Ndazungulira paliponse kufunafuna choonadi ndi chilungamo.” “Choonadi ndi chilungamo?” “Inde.” “Chatani? Kodi mumapemphera?” “Ayi. Siine nkhosa yampingo wanu. Koma kungoti mbalame yotopa imatera pamtengo uliwonse kuti ipume. Ndafufuza m’misika, m’mashopu, m’mphambano, m’minda, m’makhoti ngakhalenso m’tchire. Ndayenda ine. Ndakwera m atatu, ngolo, mabasi, malole, sitima komanso maboti. Ndapitapo kwa apolisi, oweruza komanso kumaofesi osiyanasiyana a boma. Ndapita kwa ophunzira pasukulu yaukachenjede ndiponso aphunzitsi, koma sindinapeze yankho la nkhawa yanga. Kenako munthu wina anandiuza kuti: ‘Pita kwa munthu wamulungu.’ Ndiye munthu ameneyo ndi inuyo, si choncho?” “Inde, mwabweradi kwa munthu woyenerera.” “Mumawerenga komanso kutanthauzira mawu a Mulungu. Ndiye ndikufuna ndikutulireni nkhawa yanga yomwe yakhala ikundisowetsa mtendere kwa nthawi yaitali. Sindikubisirani kanthu chifukwa sindikukayikira kuti mundipatsa malangizo enieni ochokera pansi pamtima. Kalekalelo, panali mtsikana wina. Iye anali wodzisunga pakati pa atsikana a nthanga yake. Pamoyo wake ankamvera ambuye ake awiri basi: Atate ake 149