Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 149

Matigari madzi pamene munali ndi ludzu! Anthu amenewa adzalira kuti: Kodi Ambuye tinakuonani kuti muli ndi njala, muli ndi ludzu, muli osavala, mukudwala kapena muli kundende kuti tikuthandizeni? Ndipo inu mudzawayankha kuti: Monga mmene munachitira kwa aang’ono awa pakati panu, munachitira ine amene—“ Matigari anatsukuluza kukhosi kwake. Wansembe uja anazindikira kuti mwalowa munthu ndipo anasiya kupemphera kuja n’kuimirira. Chipumi chake chinkangoti waliwale ngati malata chifukwa chathukuta lomwe linkatsika pankhope pake. Mtima wake unkagunda mwamphulupulu, koma anayesetsa kuukhazika pansi. “Ndinu ndani?” wansembeyo anafunsa Matigari. Matigari asanayankhe, wansembe uja anakumbukira pemphero lake lija komanso zomwe ananena zija, zoti anthu om- we sanathandize abale ake a Khristu adzaponyedwa ku Gehena wamoto komwe adzakakukute mano mpaka kalekale. Zimenezi zinachititsa kuti ayambe kuchita zinthu mwaulemu ndi Matigari, komabe ankachita zinthu mwamantha. “Chonde khalansi pansi!” Iye anamulozera Matigari mpando ndipo anayamba kumulonjera mwaulemu kwambiri. “Ndikudziwa kuti sindikufunikira kuchita kufunsa, koma kodi muli ndi njala?” “Osati kwenikweni.” “Kapena pali penapake pamene simukumva bwino m’thupi?” “Ayi.” “Kapenatu muli ndi ludzu, si choncho?” “Ayinso.” 148