Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 147

Matigari Yovomerezeka komanso akuvina kavinidwe komwe ndi kovo- merezeka m’dziko. Kungoyambira dzulo, ndalowa m’chipani cha anthu amantha, moti nanenso ndaphunzira kutseka kamwa langa kuti lisandilowetse m’mavuto. Mukhoza kunyamuka tsopano . . . Ayi, tadikirani kaye . . . Ndapeza mfundo inayake . . . tamvetserani. Ngati mukufunitsitsadi kupeza mayankho a ma- funso anu, pitani kwa wansembe. Iye sasiyana ndi Baibulo lake. Iye amangokhalira kuwerenga Baibulo tsiku lonse n’kumalitan- thauzira kwa anthu. Akhoza kukakuuzani zambiri zokhudza choonadi ndi chilungamo . . . ” Matigari anayang’ana mphunzitsiyo. Maso a mphunzitsiyo ankaonekeratu kuti adzadza ndi mantha. Nkhope yake inali thukuta lokhalokha. “Ndikufuna ndikutsineni khutu pang’ono,” anatero Matiga- ri. “Ndikuchokera kwa wophunzira nyenyezi zamakono. Ndina- muuza kuti mantha akachuluka m’dziko mumachitika zoipa zambiri . . . koma si zokhazo. Pali magulu awiri a anthu ophunz- itsa nyenyezi zamakono: Omwe amakonda choonadi, komanso ena omwe amachigulitsa.” 146