Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 146
Matigari
“Ndiye kuti simundiuza kumene ndingapeze zimenezi?”
“Kupeza chiyani? Khatelo?”
“Choonadi komanso chilungamo. Pamene tinali kundende
kuja, kodi si paja ndinakumvani mukufunsa kuti: ‘Ngati sind-
ingaphunzitse choonadi, ndiye ndiziphunzitsa chiyani?’”
“Kungochokera pamene tinasiyana dzulo lija, tulo sindina-
tione mpang’ono pomwe. Sindinapumenso ngakhale pang’ono.
Ndakhala ndikuzungulira m’dzikoli kuti ndipeze munthu ame-
ne angandiuze kumene munthu yemwe wadzimanga ndi lamba
wamtendere angapeze choonadi ndi chilungamo! Ndinalowa
m’tchire ndipo ndinakumana ndi mayi wina yemwe anandiuza
kuti: ‘Pita kwa amene amaphunzitsa nzeru zamakono, anthu
omwe amaphunzitsa nyenyezi zamakono!’ N’chifukwa chake
ndabwera kwanu kuno. Tengani choko chanu kapena cholem-
bera chanu mundiuze: Kodi ndi kuti m’dziko muno kumene
munthu amene wadzimanga ndi lamba wamtendere angapeze
choonadi ndi chilungamo?”
“Shiiiiiiiiii! Musamayankhule mokweza kwambiri,” mphunzitsi
uja anamuchenjeza Matigari. “Kumbuyo kulibe maso, zimene
zachitika dzulo zija tiyeni tiziiwale. Lero ndi tsiku lina.
Mawanso lidzakhala losiyana ndi lero. Kodi simunamve kuti
aphunzitsi komanso mapulofesa akumamangidwa popanda
kuzengedwa mlandu? Tandiyang’anani ineyo. Ndili ndi mkazi
komanso ana awiri. Kodi azidzadya chiyani ndikamangidwa
n’kukatsekeredwa kundende? Zoona ndimangidwe n’kuzunz-
itsa anthu osalakwa chifukwa chokonda kufunsa mafunso basi?
Wakuba tinatsekeredwa naye dzulo uja ananena kuti, ‘Munthu
wanzeru ndi amene amadziwa kutseka pakamwa pake.’ Ana-
wonjezeranso kuti pali anthu ena omwe amapindula m’moyo
kokha chifukwa choti akuimba nawo nyimbo yomwe ndi
145