Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 142

Matigari Gawo 14 Wophunzira anali atabindikira kwayekha kwinaku aku- werenga. Atangomuona Matigari, anayamba kunjenjemera moti buku lomwe anagwira m’manja mwake linagwera pansi. Sana- peze mphamvu zouza Matigari kuti akhale pansi. “Mwabwera kudzatani kuno? Mwabwera kudzatani?” wophunzirayo anafunsa Matigari akuchita mantha kwambiri. Matigari anaima kaye phee. Anayamba kuganizira kuti kodi wophunzira ameneyu ndi yemwe uja amene ndinatsekeredwa naye limodzi m’ndende? Kodi chamuchitikira n’chiyani kuti ayambe kuchita mantha chonchi n’kusiya nthabwala komanso kulimba mtima kwake kuja? Kodi mtima wake wangati wa mkango uja walowera kuti? Kenako Matigari anayamba ku- mufotokozera zimene anabwerera. “Ndayendayenda paliponse m’dziko lino kufunafuna choonadi ndi chilungamo. Ndinakumana ndi mzimayi m’then- gomu ndipo anandiuza kuti: ‘N’chifukwa chiyani wasiya wophunzira nyenyezi zamakono?’ Zimenezo zinandikumbutsa za iweyo, ndinakumbukira kuti tinamangidwira limdzi muselo ija dzulo. Ndiyeno ndinadziuza kuti: ‘Inde, si wophunzira uja anamangidwa chifukwa chofunafuna choonadi?’ Ndinaona kuti ndiyambirenso kufufuza kwanga. Munthu sayenera kunyozetsa mphamvu zafumbi limodzi kapena dontho limodzi lamvula. N’chifukwa chake ndakupeza kuno. Tsegula mabuku omwe ukuwerengawo ndipo undiuze: Kodi ndi kuti kumene munthu amene wadzimanga ndi lamba wachilungamo angapeze choonadi ndi chilungamo m’dziko lino?” “Tamvetserani,” anatero wophunzira uja, akunjenjemerabe komanso mantha atamusungunura, “Masiku ano dziko linamera mano, zinthu zinasintha. Kodi mwamva chilengezo chomwe 141