Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 140

Matigari ndi chilungamo ndi chintchitodi chachikulu. Koma kaya ndi- topa chotani, sindisiya kufufuza. Sindingalole kuti ndisiye John Boy mesenjala, komanso mtsamunda, omwe ali ngati nthata zo- yamwa magazi, kuti atenge nyumba yomwe ndinavutika kui- manga ndi manja angawa. Zingatheke bwanji kuti ndimusiye atenge nyumba yomwe ndinaikhetsera magazi anga? Ndinga- lolelenji kuti chuma changa chonse chikhale m’manja mwa an- thu omwe amakolola pamene sanalime komanso mamesenjala awo achikuda omwe ndi adyera? Nkhani inanso yomwe inamupatsa mangolomera ndi ya zimene Guthera komanso Muriuki anachita kuti amupu- lumutse. Iye anaganizira za Guthera. Kenako anaganizira za Muriuki. Ululu womwe anthuwa ankamva unasandukano wake; mavuto omwe ankakumana nawo, anasandukanso ake. Ankati akakumbukira kuti Guthera anadzipereka ngati nkhosa yoperekedwa nsembe kuti amupulumutse, ankamva ululu woopsa mumtima mwake ndipo maso ake ankayamba ku- yabwa atalengeza misozi. Iye anadzifunsa mobwerezabwereza kuti: “Kodi ndi kuti, ndi kuti padzikoli komwe choonadi ko- manso chilungamo chikubisala? Kodi ana anga akhala aku- zunzika mpaka liti, kusowa pokhala, kuyenda osavala komanso kugona ndi njala? Nanga kodi ndi ndani amene angapukute misozi ya azimayi omwe analandidwa malo awo ngati mayi anakumana naye m’tchire uja?” Ayi! M’chilengedwemu komanso m’mbiri yonse ya anthu muyenera muli yankho, Matigari analingalira mozama. Iye ankafunika kupeza munthu yemwe angamasule mfundo yomwe yamangidwa pamene pali yankholo, munthu yemwe angaulule chinsinsi cha m’chilengedwe. 139