Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 138

Matigari “Mukapitiriza kuchita zimenezi, mapeto ake mufika pamene ndafika inepa—kumatola zinyalala kwinaku ukuyankhula wekha ngati wamisala! Anatero mayiyo mokweza kwambiri ngakhale kuti Matigari anali ataima pafupi naye. ‘Mukuyang’ana chiyani m’tchire muno?’” “Ndikufufuza choonadi ndi chilungamo,” anatero Matigari. Mayiyo anaseka, ankaseka mokhala ngati akumumvera chi- soni komanso pa nthawi imodzimodziyo mokhala ngati akumunyoza, ndipo kenako anamupatsa madzi akumwa aja. “M’bale wanga woyendayenda, sungapeze mayankho a ma- funso ako m’tchire muno, chifukwa simukhala anthu. Choonadi ndi chilungamo chimapezeka m’zochita za anthu. Cholondola ndi cholakwika chimaoneka m’zimene anthu amachita. Koma ngakhale pakati pa anthuwo, ukhoza kuvutika kwambiri kuti upeze mayankho a mafunso ako. Ukudziwa chifukwa chake? Le- ka ndichite kukunong’oneza zimenezi, ena angatimvere. Paja nayonso mitengo ili ndi makutu. Tayandikira. Nd i m antha. M’dziko muno mwachuluka anthu amantha. Kodi mwambi uja umati chiyani paja? Mantha akachuluka m’dziko mumachitika zoipa zambiri. Ndisiyeni ine mumtendere. Nyamukani bambo, pitani kwa anthu anzeru, kwa anthu omwe amadziwa kupenda nyenyezi.” “Kodi anthu amenewo amapezekabe masiku ano?” anafunsa Matigari. “Inetu ndimaganiza kuti abusa aziweto ndiye anthu anzeru, chifukwa nthawi zambiri amakhala akupenda nyenyezi. Nyenyezi zinkawatsogolera akamayenda m’zipululu komanso m’tchire. Ndi nthawi imene ankayendayendayi yomwe anapeka nyimbo yodzadza ndi nzeru zochokera kwa nyenyezi. Koma si amene ndangokumana nawo posachedwapa ataunjikana n’ku- mamvetsera wailesi, Wailesi ya Choonadi kuti iwathandize 137