Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 137

Matigari Gawo 12 Iye anayamba kuyang’ana choonadi ndi chilungamo mu udzu komanso m’tchire. Iye anayang’anayang’ana m’minga, zi- yangoyango, m’mikwaso, zulu komanso m’zisa za mbalame. Iye anayang’anayang’ana m’chilengedwe chonse cha m’tchiremo. Ankangokhala ngati wachita misala. Koma kenako mtima wake unayamba kugunda kwambiri. Iye anaganiza kuti: “Mlimi sasiya kufesa mbewu chifukwa choti mbewu ina sinamere. Wofunafu- na chilungamo satopa mpaka atachipeza. Choonadi sichiwola kapena kufwifwa. Chilungamo chimaposa mphamvu. Tandiuza- ni: ‘Kodi n’kuti kumene munthu angapeze choonadi ndi chi- lungamo m’dzikoli?’” Kenako atafika m’chigwa china, anakumana ndi abusa a zi- weto. Atawayandikira, anazindikira kuti abusawo anali ndi mawailesi awiri. Ina ya Sanyo ndipo ina ya Phillips. Mawailesiwo anawakweza mogonthetsa mkutu. Onse ana- watchera pasiteshoni yofanana. Mwatsegulayi ndi Wailesi Yanu ya Choonadi . . . Pulezidenti wadziko lino . . . “Zoona kumvetsera wailesi ntchire ngati muno?” Wailesi ya Choonadi inali italowa m’malo mwa zitolilo zomwe abusa amaimba akamafuna kugoneka nkhosa. Kenako anatembenuka n’kuwasiya abusawo ndipo anayamba kulowera kwina komwe sankakudziwa. Zimene zinkamveka pamawailesi aja zinkango- khala ngati zikumupirikitsa kuti achoke m’chigwacho . . . Kenako anakumana ndi mayi wachikulire akuchotsa zinyalala panja pakansasa kake komwe kanali m’tchiremo. Tsitsi la mayiyo linkangooneka ngati chikusa. Zinkaoneka kuti panali patatha zilimuka chipeso chisanadutsemo. Matigari anapita kwa mayiyo n’kumupempha madzi akumwa kuti aphe chipemba. 136