Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 136

Matigari ndi cholakwika? Kodi woipa ndi ndani? Kodi ndi amene wachititsa kuti munthu wina achite tchimo, kapena amene wachita tchimoyo? Kodi wolakwa ndi ndani? Kodi ndi amene wachititsa kuti wina ayambe kuyenda njira yolakwika, kapena amene wagwidwa akuchita cholakwikacho? Kalekalelo, ana ankaimba pogwiritsa ntchito zala za m’manja. Ankati: Chala chaching’ono chinati: Tiye tizipita! Chala chachiwiri chinati: Kuti? Mgonapakati anati: Tikabe? Msonyaalendo anati: Nanga tikakagwidwa? Mteketeke anati: Ine toto, sindipita nawo. Kodi n’chiyani chimene chinafunika kukonzedwa choyamba? Zinthu zimene zikuchititsa kuti munthu achite tchimo, kapena miyoyo ya anthu omwe akuchita tchimolo?” “Kodi choonadi ndi chilungamo chabisala kuti pamoyo wa munthu?” Iye ankadzimva wosungulumwa. Maganizo oti angochita zinthu zoti zimuthandize kuti adzipulumutse n’kuiwala zonse, anamugwira nsukunyu n’kumufoola. Kenako anango- khala ngati wapenga, moti anasiya kuyenda munsewu muja n’kulowa m’tchire. 135