Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 133

Matigari Ophunzira awiri apasukulu yaukachenjede anamangidwa dzulo atapezeka ndi mabuku oletsedwa m'dziko muno . . . Ophunzira enanso anamangidwa atagwidwa akuchita ziwonetsero zosonyeza kusagwirizana ndi zimene boma la United States komanso mayiko ena a ku Ulaya akuchita pothandiza boma la ulamuliro watsankho la ku South Africa. Ophunzira amenewa agamulidwa kuti akakhale kundende zaka zisanu. Pamene ophunzirawa amatengedwa n'kumapita kujere anayamba kukuwa kuti: Chipambano ndi chathu! Wophunzira yemwe amafuna kuyambitsa chipani chake wauzidwa kuti asiye kulitokosola dala boma . . . M'dziko muno muli chipani chimodzi chokha basi. N'chifukwa chiyani ophunzirawa akufuna chipani china? Mtsogoleri wa dziko lino, Pulezidenti Ole, wanena kuti ophunzira amenewa ayenera kukhala okhutira ndi chipani chimodzi chimene chili mā€™dziko muno, chomwe ndi chipani cholamula. Nduna Yoona Zachilungamo yayambapo ulendo wake woyendera midzi ya m'dziko muno. Zikunekanso kuti ikachezera kampani ya An- glo-American Leather and Plastic Factory. Ikapita kumeneku ikakambi- rana ndi oyendetsa kampaniyi komanso ogwira ntchito. Pafakitaleyi panachitika chipwirikiti dzulo pamene apolisi amalimbana ndi ogwira ntchito omwe amachita ziwonetsero. Ogwira ntchito omwe anakwiya ndi kuchepa kwa malipiro anawotcha ziboliboli za oyendetsa kampani- yi. Malipoti akusonyeza kuti apolisi akanapanda kulowererapo, ndiye kuti ogwira ntchitowo akanaimbidwa mlandu woopsa woononga ko- manso kuwotcha zinthu mwadala. Zimenezi zikanachitika ndiye kuti chuma cha dziko lino chikanakhudzidwa kwambiri. Chidziwitso chapadera . . . chidziwitso chapadera . . . Mneneri wa boma wanena kuti anthu asamamvetsere zomwe ena akunena zoti mngelo Gabrieli watulutsa akaidi mndende ina komanso kuti mkaidi m'modzi anali Yesu Khristu. Iye anati zimene anthu akufalitsazi zoti Yesu kapena Gabrieli wabweranso ndi bodza lankunkhuniza. Boma 132