Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 129
Matigari
"Kungoti nyuzipepalayi sinanene zinthu zambiri. Anthu
akumanena kuti kunamveka mabingu komanso kunachita
ziphaliwali pa nthawi imene zimenezi zimachitika! Aliyense
amaganiza kuti kugwa mvula, koma sikunagwe dontho ngakha-
le limodzi. Ndipo mosadziwika bwino, mabingu komanso
ziphaliwali zija zinasiya."
"Ndi ndani akudziwa, mwina ndi ziphaliwalizo zomwe zi-
natsegula zitseko zandendeyo? Komansotu akuti chitsekocho
anachipeza mmene chinalili chosathyoka kapena kupindika
paliponse. Komanso makoma anali mmene analili."
"Zimenezitu ndi zodabwitsa kwambiri. N'chifukwa chiyani
anthu ena amanena kuti zozizwitsa sizichitika? Amafuna ataona
chiyani kwenikweni?"
"Mukudziwa, anthu ena akamaliza kuwerenga zozizwitsa
zonse zomwe Mose anachita amaganiza kuti zimenezo zango-
khala nthano chabe za m'Baibulo."
"Zoona, zozizwitsa zimachitikadi. Tsiku lina ndinaona mun-
thu akutulutsa nkhunda m'chisoti chake komanso akutulutsa
ndalama zapepala za ma 5 Shillings kuchokera mumphuno mwa
mwana wazaka zitatu."
"Basi siyani nkhani zabodzazo! Mmene ichepera mphuno ya
mwana wazaka zitatumo n’kutuluka 5 Shillings? Zafodya basi!
Chinthu chimene ndikulakalaka nditadziwa n'choti, kodi Matig-
ari ndi ndani kwenikweni?"
"Kodi simunamve zoti Baibulo limanena kuti adzabweranso
kachiwiri?"
"Kodi mukutanthauza kuti ndi uja aneneri ananena kuti
adzabweranso? Mwana wa Munthu?"
128