Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 126

Matigari “Zimenezo ndi zimene Matigari ma Njiruungi amanena: ‘Azungu nonse komanso atchito anu onse, ukooo! Dzikoli lili ndi eni ake.’” “Koma ndiye anawauza chilungamotu!” “Zoonadi.” “Inde zoona, choonadi chenicheni.” “Ine ndakhala ndikunena kuti: Kodi anthu osakonda dziko lawowa adzapita kuti anthu omenyera ufulu wadziko lathu akadzabwerera, akubangula ngati mikango n'kumanena kuti: ‘Ife okonda dziko lathu tabwera! Nonse ogulitsa dziko lathu chokani!’” “Kodi ndi zoona kuti zinthu zidzasinthiratu? Koma ngati zinthu zitapitirira mmene zililimu bola kukayembekezera ku- manda ndithu. Zoona anthu obwera, kaya ndi a ku Ulaya kapena ku Amerika, azipeza malo omanga mahema awo, ma- hema oti asungiremo zida zankhondo, mahema oti azisungira- mo zinthu zomwe atibera, ife eni ake anthu akuda tikusowa pokhala? Komanso mabwana achikuda kwinaku atatanganidwa kusokoneza maganizo a anthu ndi lilime lokha uchi komanso pogwiritsa ntchito apolisi kuti azitseka anthu pakamwa powazunza?” “Nawenso wanena zofanana ndi mfundo zoluma ndi choonadi zomwe Matigari ananena. Matigari ndi wosagonjet- seka chifukwa atangomumanga anawauza kuti: ‘Musasangalale chifukwa choti mwandiponyera kudzenje lamdima. Mundionan- so ndikutulukira pakangotha masiku atatu.’” “Tatiuzeni nthuni! N'chifukwa chiyani Matigari ma Njiruun- gi sanabwere kuminda kuno? Akanabwera ndikanamuuza kuti: Musabwerere m'mbuyo . . .” 125