Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 125

Matigari atangofika pagetiyo mahatchiwo anangoima chii. Iwo anaye- setsa kuwamenya kuti aziyenda, koma mahatchiwo sana- wamvere mpang’ono pomwe chifukwa cha mantha.” "Zimangokhala ngati zimene inachita hatchi yomwe inaona mngelo wa Ambuye ataima pamsewu ija?" "Sinalitu hatchi, anali bulu!" "Mukanganabe tikamaliza, pano tikufuna timve kaye nkhani ya Matigari!" "Kenako anamuona ataima pakati pamsewu, mkono wake umodzi uli m'chiunomu. Winawo atanyamula lupanga loyaka moto." "Mwamva zimene wanenazo! Lupanga loyaka moto!" "Kenako anawauza kuti: 'Ndinu nthata zoyamwa ena maga- zi! Ndibwezereni makiyi a nyumba yanga komanso mundibwe- zere malo omwe munalanda abale anga!'" "Tabwerezanso! Mwati ananena kuti chiyani? Anati azungu onse komanso nthata zachikuda zichite chiyani?" "Anati abweze chuma chomwe anaba kwa eni ake!" "Zimenezotu ndi zoona. Anawachita bwino anthu osayamika amenewa omwe amangokhalira kutipondereza. Anthu amenewa akhala akutikama mkaka kwa nthawi yaitali. Dzulo anali azungu obwera limodzi ndi antchito awo. Leronso ndi omwewo akutizunza, kungoti avala nkhope zina. Kulikonse ungalowere, kaya ndi kumafamu, kaya kumafakitale, ukawapeza ali phathi- phathi, bwana ndi wantchito wake. Kodi anthu omwe timavuti- ka kugwira ntchitofe tidzamera liti mnofu wabakha, tidzamwa liti tiyi wamkaka?" 124