Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 122

Matigari “Mantha. Mantha akachuluka m’dziko zotsatira zake zima- khala mavuto osaneneka.” ”Mawuwa ndi amene Matigari anawauzanso anthuwo.” “Munthu wochepa thupi komanso wamfupi n’kulimba mti- ma choncho? Mwamunadi ndi mumtimamu, kokha mchepera wa kalulu!” “Kodi mwanena kuti ndi wamfupi? Inetu ndamva zoti ndi chiphanza, munthu wamphamvu zake. Ndi wamtali zedi moti akhoza kugwira mitambo!” “Mwati bwanji?” “Inde, ndi wamtali ngati nsungwi moti mutu wake umagun- da kumwamba!” “Musandiuze atsikana! Kenako chinachitika n’chiyani?” “Kodi n’chiyaninso chimene ndingakuuzeni amwali chomwe simunamve? Kenako, atayamba kuyenda, imvi zake komanso makwinya omwe anali pamphumi pake zinabalalika. Chithunz- ithunzi chake chinayamba kutalika n’kumalowera cha uko. ‘Tamusiyani mtsikanayo msanga! N’chifukwa chiyani mukuzun- za mayi wadziko lino!’ Anawauza choncho apolisiwo. ‘Tangoyerekezani kutambasula dzanja lanu n’kumukhudza muone!’” “Oh, musandiyendetse thupi mache, zoona anthu omenyera ufulu wadziko lathu lino adakalipo! Koma samachita mantha?” “Kuchita mantha n’chiyani? M’mabukutu mwa anthu ome- nyera ufulu mulibe mawu akuti ‘mantha.’ Simungakhulupirire nditakuuzani kuti anabwerezanso kuwachenjeza apolisiwo kuti: ‘Tangoyerekezani kumukhudza mtsikanayo muone! Mudziwa kuti mukusewera ndi munthu wotani. Mundidziwa ine Matigari ma Njiruungi!’” 121