Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 118

Matigari Gawo 5 Iye anapita m’malo ogulitsira zakudya. Anthu ankachita chidwi kwambiri ndi nkhani ya Matigari moti ena anaiwaliratu kumwa ntenthandevu wawo komanso kudya chakudya chawo. Iwo anangokhala n’kumamvetsera, makutu ali petupetu m’mwamba. “Ndi Ngaruro wa Kiriro amene anayamba kumuzindikira.” “Ngaruro wa Kiriro? Ndakhalatu ndikunena ine kuti Nga- ruro wa Kiriro ndi wozindikira komanso amaona patali.” “Mwana uja ali ndi nzeru zachibadwa.” “Koma kumenekooo! Patsogolo ndi ndani? Patsogolo ndi Ngaruro wa Kiriro!” “Kodi mukudziwa zimene zimachitika pamene Ngaruro wa Kiriro amayankhula pamsonkhanowo? Mitima ya anthu onse imanyamuka m’malele moti zimangokhala ngati aliyense wad- zozedwa usilikali. Aliyense anali wokonzeka kunyamula zida n’kuyamba kulimbana ndi anthu oponderezawa. Mawu ake anali otsitsimula komanso olimbikitsa zedi moti ngakhale mun- thu akanakhalira mbaula yoyaka moto sakanazindikira kuti akupsa. Iye anati: ‘Tayani kutali mantha anu chifukwa sitili to- kha! Abale athu omenyera ufulu wadziko lathu abweranso.’ Zimenezo ndi zimene anawauza. Anawafotokozeranso mwatsa- tanetsatane zimene zinachitika kuti akumane ndi Matigari ko- manso mmene Matigari amayankhulira m’mafanizo komanso m’miyambi kuti: ‘Phindu liyenera kubwerera kwa ife anthu om- we timakhetsa thukuta m’dziko muno.’ Iye ananenanso kuti an- thu opondereza anzawo komanso amene amawayang’anira ayenera kupakila nsanza zawo n’kuona msanawanjira. Ngaruro wa Kiriro anawafunsa kuti: Kodi eni ake a dzikoli ndi ndani? Og- wira ntchito onse anayankhira limodzi kuti: ‘Ndi ifeeee! 117