Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 116

Matigari ‘Lolani ana adze kwa ine.’ Koma anawo anachita mantha kwam- biri moti anangotembenuka n’kulangiza mapazi. Ndi mwana m’modzi yekha amene anamutsatira.” “Ndikuuzeni anthuni, si bwino kumanyoza munthu kapena kumuchitira chipongwe kokha chifukwa cha mmene wavalira komanso mmene akuonekera. Sizidalira kuti munthu akhale chiphanza kuti akhale mpulumutsi. Ndikanasangalala kwambiri ndikanakumana naye pamasompamaso. Ndikanakonda n’kana- muona pompano kuti ndimugwire chanza . . . ” Ndiyeno Matigari anatulukira pafupi ndi gulu la anthulo n’kuima pakhonde. “Abale anga tandiuzeni chonde. Kodi ndi kuti m’dziko muno kumene munthu angapeze choonadi komanso chilungamo?” Anthuwo anangoti chetee n’kumangomuyang’ana ndi diso la nkhwezule. Ankamuyang’ana monyodola kwambiri ngati mmene munthu angayang’anire wamisala yemwe akuvina mosagwirizana ndi nyimbo imene yafika pakolasi n’ku- masokoneza anzake. Kenako anayamba kuyankhulana n’ku- madandaula kuti munthuyo akuwaonongera nyimbo yawo yomwe inali itafika pa tiso we. “Kodi munthu ameneyu akunenanso chiyani?” “Nayenso ndi wopanda nzeru bwanji, zoona angatisokoneze tikukambirana nkhani yofunikayi pomafunsa mafunso opanda mchere?” “Bwanji akuleka kungopita ku Wailesi ya Choonadi kuti aka- funse?” “Akhoza kupita kwa Nduna Yoona Zachilungamo ngati aku- funa kumva zambiri.” 115