Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 115

Matigari Gawo 4 Matigari anapita m’malo ogulitsira malonda. Anazungulira ponseponse pomwe akanapeza anthu. Anapita kwa ogulitsa m’magolosale komanso kwa ogula malonda omwe ankadzadza m’mashopu komanso m’makonde ake akukambirana nkhani . . . “Ana ndi amene anali oyambirira kumuona.” “Ana? Ndiye kuti anawauza anawo kuti iyeyo ndi Matigari? Pajatu mwana ndi mfumu sasiyana zochita, amagwirizana kwambiri. Komatu paja ana ndi ana basi, amaluma bere lomwe likuwayamwitsa!” “Bwanji? Anachitanso chiyani?” “Eti anayamba kumugenda. Anamubongetsa nayo miyala.” “Kumugenda? Koma amadziwa kuti munthu akumu- gendayo ndi ndani?” “Ayi.” “Koma nawonso ana amasiku ano! Bwanji osachita manyazi kugenda munthu wamkulu! Nanga akanamuchotsa diso?” “Pamenepo ndi pamene pali podabwitsa. Mwalatu ngakhale umodzi sunamukhudze.” “Musakhaletu mukuchulukitsa nkhaniyi ndi malovu! Mwati bwanji?” “Miyalayo imati ikamamuyandikira, imangosanduka nkhun- da n’kuuluka.” “Nkhunda?” “Inde! Mukuganiza kuti zimenezi zingangochitika?” “Anawo anayamba kuchita mantha. Kenako kunabwera an- thu ena n’kuyamba kuwafunsa kuti: ‘N’chifukwa chiyani muku- genda munthu wachikulileyu?’ Koma Matigari anati: 114