Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 110

Matigari Matigari ma Njiruungi. Mwatsegulayi ndi Wailesi Yanu ya Choonadi . . . Mtsogoleri wa dziko lino Pulezidenti Ole analandira ndalama zokwana 50 Shillings kuchokera kwa anthu ena abizinezi dzulo. (Akuda ndi azungu omwe). Anthuwo anapita kukakumana naye kunyumba kwake. Ndalama imene anaperekayo ndi yoti ipite kuthumba la apulezidenti lothandiza ana olumala. Mtsogoleri wa amalondawo anayamikira Pulezidenti Ole pothetsa chisokonezo chomwe asilikali anayambitsa ponyanyala ntchito ati chifukwa izi zikanachititsa kuti m’dziko muno musakhale bata ndi mtendere . . . Aphunzitsi ena a sukulu yaukachenjede anakaonekera kukhoti dzu- lo chifukwa chopezeka ndi mabuku a Karl Marx komanso V. Lenin om- we anasindikizidwa ku China. Mabuku onsewa ndi onena za ufulu wa ogwira ntchito, ndipo makamaka omwe anasindikizidwa ku China ndi oletsedwa m’dziko muno kungochokera pamene tinalandira ufulu wodzilamulira . . . Ophunzira asanu a kusukulu yaukachenjede amangidwa dzulo popanga nawo ziwonetsero panja pa maofesi a kazembe wa ku Britain komanso United States. Ophunzirawa anachita ziwonetserozi posonye- za kusagwirizana ndi zimene mayikowa akuchita pothandiza boma latsankho la ku South Africa. Zimene anachitazi ndi zoletsedwa chifu- kwa pulezidenti wa dziko lino ananena kuti pasapezeke munthu wochi- ta ziwonetsero m’dziko muno. Lipoti lina lochokera ku Johannesburg, South Africa, lanena kuti anthu ena omenyera ufulu wawo achipani cha ANC ndi amene akugan- iziridwa kuti anaika bomba muhotela ina yomwe azungu amakonda kupitako. Azungu a m’dzikoli anena kuti akuchita mantha kwambiri ndi zigawenga za SWAPO komanso ANC . . . 109