Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 107

Matigari Kenako anamva munthu akutsegula zitseko zomwe zinali m’njira yolowera kuseloyo ndi makiyi kuti kolokochokolokocho. Ankadzifunsa kuti: ‘N’chifukwa chiyani wapolisi akuyenda mo- zemba choncho mumdima, osayatsa magetsi?’ Onse anachita mantha aakulu. Kenako anamva kutsegula pakhomo laselo lawo lija. Pa nthawiyi aliyense anali ndi mantha ndipo anakonzeka kuti akumana ndi zoopsa. Kenako anamva mawu chapansipan- si. “Tulukani nonse. Osapanga phokoso komanso osayang’ana m’mbuyo! Mukafika mumsewu, iwe Matigari, ukadikire pafupi ndi chipatala chija. Enanu mukapitirize kuyenda osayang’ana m’mbuyo!” Onse anatuluka mwakachetechete ndipo chifukwa cha mdi- ma anafufuza khomo n’kutuluka. Makomo onse anali otsegula ndipo pamalo ofikira alendo panalibepo munthu aliyense. Ankangokhala ngati akulota! Ena ankangoganiza kuti akuona masomphenya. Iwo anatulutsidwa m’ndendeyo ndi munthu yemwe sanamuone. Ndiye pamene ankayenda n’kumalowera chakumsewu, ambiri ankadzifunsa kuti: ‘Kodi Matigari ma Njiruungi, munthu wotha kutsegula zitseko za ndende, ndi ndani kwenikweni?’ Kungochokera tsiku limenelo, mbiri ya Matigari inabuka ngati moto ndipo inafalikira m’dziko lonse. Iye anakhala mpulumutsi. Anthu anayamba kumugomera. Koma ambiri ankadzifunsabe kuti: ‘Kodi Matigari ma Njiruungi ndi ndani?’ 106